NYIMBO YA SOLOMONI8nya_bib

1Ukanakhala kuti ndiwe mlongo wanga,amene anayamwa mawere a amayi anga!Ndikanakumana nawe pa njira,ndikanakupsompsona,ndipo palibe wina aliyense akanandinyoza.2Ndikanakutengandi kukulowetsa mʼnyumba ya amayi anga,amayi amene anandiphunzitsa,ndikanakupatsa vinyo wotsekemera kuti umwe,zotsekemera za makangadza.3Mutu wanga watsamira dzanja lake lamanzerendipo dzanja lake lamanja landikumbatira.4Inu akazi a ku Yerusalemu, ndithu ndikukupemphani:musachigwedeze chikondi kapena kuchiutsampaka pamene chifunire ichocho.5Kodi ndani uyo akutuluka ku chipululuyo,atatsamira wokondedwa wakeyo?MkaziNdinakudzutsa pa tsinde pa mtengo wa apulosi,pamenepo ndi pamene amayi anachirira,pamenepo ndi pamene wokubereka anamva ululu pokubala iweyo.6Undiyike pamtima pako ngati chidindo,ngati chidindo cha pa dzanja lako;pakuti chikondi nʼchamphamvu ngati imfa,nsanje ndiyaliwuma ngati manda.Chikondi chimachita kuti lawilawingati malawi a moto wamphamvu.7Madzi ochuluka sangachizimitse chikondi,mitsinje singachikokolole chikondicho.Ngati wina apereka chuma chonsecha mʼnyumba mwake chifukwa cha chikondi,adzangonyozeka nazo kotheratu.8Ife tili naye mlongo wathu wamngʼono,koma alibe mawere,kodi tidzamuchitira chiyani mlongo wathuyupa tsiku limene adzamufunsire?9Ngati iye ndi khoma,tidzamumangira nsanja ya siliva.Ngati iye ndi chitseko,tidzamutchinga ndi matabwa a mkungudza.10Ine ndili ngati khoma,ndipo mawere anga ndi nsanja zake.Tsono mʼmaso mwa bwenzi langandine wobweretsa mtendere.11Solomoni anali ndi munda wampesa ku Baala-Hamoni;iyeyo anabwereketsa munda wamphesawo kwa alimi,aliyense mwa iwo ankayenera kuperekandalama zasiliva 1,000 mʼmalo mwa zipatso zake.12Koma munda wanga wampesa ndi wangawanga ndiponso wa ine ndekha.Iwe Solomoni, khala nazo ndalama zasiliva 1,000ndipo ndalama zasiliva 200 ndi za amene akusamalira mundawo.13Iwe amene umakhala mʼmindauli pamodzi ndi anzako,ndilole kuti ndimve liwu lako!14Fulumira wokondedwa wanga,ndipo ukhale ngati gwapekapena mwana wa mbawalawothamanga mʼmapiri mʼmene mumamera mbewu zokometsera chakudya.