MASALIMO1nya_bib
1Wodala munthuamene satsatira uphungu wa anthu ochimwa,kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa,kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.2Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehovandipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.3Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi,umene umabereka zipatso zake pa nyengo yakendipo masamba ake safota.Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.4Sizitero ndi anthu oyipa!Iwo ali ngati munguumene umawuluzidwa ndi mphepo.5Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo,kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.6Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama,koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.