MIYAMBO22nya_bib

1Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;onsewa anawalenga ndi Yehova.
3Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4Mphotho ya munthu wodzichepetsandi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6Mwana muzimuphunzitsa njira yake,ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7Wolemera amalamulira wosauka,ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,adzakhala bwenzi la mfumu.
12Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13Munthu waulesi amati,“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.

Malangizo a Anthu Anzeru

17Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.18Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwakondi wokonzeka kuziyankhula.19Ndakuphunzitsa zimenezi lerokoma makamaka uziopa Yehova.20Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatuokuchenjeza ndi okupatsa nzeru,21malangizo okudziwitsa zolungamandi zoonandi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,23pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawondipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtimandipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya25kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zakendi kukodwa mu msampha.
26Usakhale munthu wopereka chikolekapena kukhala mboni pa ngongole;27ngati ulephera kupeza njira yolipiriraadzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28Usasunthe mwala wamʼmalire akalekaleamene anayikidwa ndi makolo ako.
29Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?Iye adzatumikira mafumu;sadzatumikira anthu wamba.