1Mʼmasiku otsiriza,phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsakukhala lalitali kuposa mapiri ena onse.Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.2Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti,“Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova,ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.Iye adzatiphunzitsa njira zake,ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”Malangizo adzachokera ku Ziyoni,mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.3Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambirindipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe.Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasundiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,kapena kuphunziranso za nkhondo.4Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesandi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu,ndipo palibe amene adzawachititse mantha,pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.5Mitundu yonse ya anthuitha kutsatira milungu yawo;ife tidzayenda mʼnjira za YehovaMulungu wathu mpaka muyaya.
Cholinga cha Yehova
6“Tsiku limenelo, Yehova akuti,“ndidzasonkhanitsa olumala;ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwandiponso amene ndinawalanga.7Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehovakuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.8Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga,iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni,ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe;ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”9Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula,kodi ulibe mfumu?Kodi phungu wako wawonongedwa,kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?10Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,ngati mayi pa nthawi yake yobereka,pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzindandi kugona kunja kwa mzindawo.Udzapita ku Babuloni;kumeneko udzapulumutsidwa,kumeneko Yehova adzakuwombolamʼmanja mwa adani ako.11Koma tsopano mitundu yambiri ya anthuyasonkhana kulimbana nawe.Iwo akuti, “Tiyeni timudetse,maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”12Koma iwo sakudziwamaganizo a Yehova;iwo sakuzindikira cholinga chake,Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.13“Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo;ndidzakupatsa ziboda zamkuwandipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.”Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova,chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.