MIKA1nya_bib

1Yehova anayankhula ndi Mika wa ku Moreseti pa nthawi ya ulamuliro wa Yotamu, Ahazi ndi Hezekiya, mafumu a ku Yuda. Awa ndi masomphenya amene iye anaona onena za Samariya ndi Yerusalemu.2Tamverani, inu anthu a mitundu yonse,mvetsera iwe dziko lapansi ndi okhala mʼmenemo,pakuti Ambuye Yehova achitira umboni wokutsutsani,Ambuye akuyankhula ali mʼnyumba yake yopatulika.

Chiweruzo cha Samariya ndi Yerusalemu

3Taonani! Yehova akubwera kuchokera ku malo ake;Iye akutsika ndipo akuponda pa malo okwera a dziko lapansi.4Mapiri akusungunuka pansi pake,ndipo zigwa zikugawikanangati phula pa moto,ngati madzi ochokera mʼphiri.5Zonsezi ndi chifukwa cha cholakwa cha Yakobo,chifukwa cha machimo a nyumba ya Israeli.Kodi cholakwa cha Yakobo nʼchiyani?Kodi si Samariya?Kodi malo achipembedzo a Yuda ndi ati?Kodi si Yerusalemu?
6“Choncho Ine ndidzasandutsa Samariya kukhala bwinja,malo odzalamo mphesa.Miyala yake ndidzayitaya ku chigwandipo ndidzafukula maziko ake.7Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya;mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto;ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake.Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere,mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”

Kulira ndi Kumva Chisoni

8Chifukwa cha zimenezi ine ndidzalira momvetsa chisoni;ndidzayenda wopanda nsapato ndi wamaliseche.Ndidzafuwula ngati nkhandwendi kulira ngati kadzidzi.9Pakuti chilonda cha Samariya nʼchosachizika;chafika ku Yuda.Chafika pa chipata chenicheni cha anthu anga,mpaka mu Yerusalemu mwenimwenimo.10Musanene zimenezi ku Gati;musalire nʼkomwe.Mugubuduzike mu fumbiku Beti-Leafura.11Inu anthu okhala ku Safiro,muzipita ku ukapolo muli amaliseche ndi amanyazi.Iwo amene akukhala ku Zanaanisadzatuluka.Beti-Ezeli akulira mwachisoni;chitetezo chake chakuchokerani.12Anthu amene amakhala ku Maroti akubuwula ndi ululu,akuyembekezera thandizo,chifukwa Yehova wabweretsa tsoka,lafika mpaka pa chipata cha Yerusalemu.13Inu anthu okhala ku Lakisimangani akavalo ku magaleta.Inu amene munayamba kuchimwitsamwana wamkazi wa Ziyoni,pakuti zolakwa za Israelizinapezeka pakati panu.14Chifukwa chake perekani mphatso zolawiranandi a ku Moreseti Gati.Mzinda wa Akizibu udzaonetsa kunamakwa mafumu a Israeli.15Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inuokhala mu Maresa.Ulemerero wa Israeli udzafikaku Adulamu.16Metani mipala mitu yanu kuonetsa kuti mukuliriraana anu amene mumawakonda;mudzichititse dazi ngati dembo,pakuti anawo adzatengedwa pakati panu kupita ku ukapolo.